Masalmo 119:157-161 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

157. Ondilondola ndi ondisautsa ndiwoambiri;Koma sindinapatukana nazo mboni zanu.

158. Ndinapenya ocita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao;Popeza sasamalira mau anu.

159. Penyani kuti ndikonda malangizo anu;Mundipatse moyo, Yehova, monga mwa cifundo canu.

160. Ciwerengero ca mau anu ndico coonadi;Ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.

161. Nduna zinandilondola kopanda cifukwa;Koma mtima wanga ucita mantha nao mau anu.

Masalmo 119