Masalmo 119:122-128 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

122. Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.

123. Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.

124. Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,

125. Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.

126. Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu;Pakuti anaswa cilamulo canu.

127. Cifukwa cace ndikonda malamulo anuKoposa golidi, Inde golidi woyengeka,

128. Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse;Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.

Masalmo 119