115. Mundicokere ocita zoipa inu;Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.
116. Mundicirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndisacite manyazi pa ciyembekezo canga.
117. Mundigwirizize ndipo ndidzapulumutsidwa,Ndipo ndidzasamalira malemba anu cisamalire.
118. Mupepulaonseakusokeram'malemba anu;Popeza cinyengo cao ndi bodza.