Masalmo 118:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Anene tsono nyumba ya Aroni,Kuti cifundo cace ncosatha.

4. Anene tsono iwo akuopa Yehova,Kuti cifundo cace ncosatha.

5. M'mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova;Anandiyankha Dandiika motakasuka Yehova.

6. Yehova ndi wanga; sindidzaopa;Adzandicitanji munthu?

7. Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza;M'mwemo ndidzaona cofuna ine pa iwo akundida,

8. Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira munthu.

9. Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira akulu,

Masalmo 118