Masalmo 115:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Aneneranji amitundu,Ali kuti Mulungu wao?

3. Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba;Acita ciri conse cimkonda.

4. Mafano ao ndiwo a siliva ndi golidi,Nchito za manja a anthu.

5. Pakamwa ali napo, koma osalankhula;Maso ali nao, koma osapenya;

6. Makutu ali nao, koma osamva;Mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;

7. Manja ali nao, koma osagwira;Mapazi ali nao, koma osayenda;Kapena sanena pammero pao,

8. Adzafanana nao iwo akuwapanga;Ndi onse akuwakhulupirira,

Masalmo 115