Masalmo 108:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu;Ndi ulemerero wanu pamwamba pa dziko lonse lapansi.

6. Kuti okondedwa anu alanditsidwe,Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutibvomereze.

7. Mulungu analankhula m'ciyero cace; ndidzakondwerera:Ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso cigwa ca Sukoti.

8. Gileadi ndi wanga: Manase ndi wanga;Ndi Efraimu ndiye mphamvu ya mutu wanga;Yuda ndiye wolamulira wanga.

Masalmo 108