6. Talakwa pamodzi ndi makolo athu;Tacita mphulupulu, tacita coipa.
7. Makolo athu sanadziwitsa zodabwiza zanu m'Aigupto;Sanakumbukila zacifundo zanu zaunyinji;Koma anapikisana ndi Inu kunyanja, ku Nyanja Yofiira.
8. Koma anawapulumutsa cifukwa ca dzina lace,Kuti adziwitse cimphamvu cace.