32. Anautsanso mkwiyo wace ku madzi a Meriba,Ndipo kudaipira Mose cifukwa ca iwowa:
33. Pakuti anawawitsa mzimu wace,Ndipo analankhula zosayenera ndi milomo yace.
34. Sanaononga mitunduyo ya anthu,Imene Mulungu adawauza;
35. Koma anasokonekerana nao amitundu,Naphunzira nchito zao: