38. Aigupto anakondwera pakucoka iwo;Popeza kuopsa kwao kudawagwera.
39. Anayala mtambo uwaphimbe;Ndi moto uunikire usiku,
40. Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri.Nawakhuritsa mkate wakumwamba.
41. Anatsegula pathanthwe, anaturukamo madzi;Nayenda pouma ngati mtsinje.
42. Popeza anakumbukila mau ace oyera,Ndi Abrahamu mtumiki wace.