Masalmo 105:38-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Aigupto anakondwera pakucoka iwo;Popeza kuopsa kwao kudawagwera.

39. Anayala mtambo uwaphimbe;Ndi moto uunikire usiku,

40. Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri.Nawakhuritsa mkate wakumwamba.

41. Anatsegula pathanthwe, anaturukamo madzi;Nayenda pouma ngati mtsinje.

42. Popeza anakumbukila mau ace oyera,Ndi Abrahamu mtumiki wace.

Masalmo 105