Masalmo 103:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Lemekeza Yehova, moyo wanga,Ndi kusaiwala zokoma zace zonse aticitirazi:

3. Amene akhululukira mphulupulu zako zonse;Naciritsa nthenda zako zonse;

4. Amene aombola moyo wako ungaonongeke;Nakubveka korona wa cifundo ndi nsoni zokoma:

5. Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino;Nabweza ubwana wako unge mphungu.

Masalmo 103