Masalmo 102:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova,Ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu;

16. Pakuti Yehova anamanga Ziyoni,Anaoneka m'ulemerero wace;

17. Anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,Osapepula pemphero lao.

18. Ici adzacilembera mbadwo ukudza;Ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19. Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ace opatulika;Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20. Kuti amve kubuula kwa wandende;Namasule ana a imfa,

Masalmo 102