Masalmo 10:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Muimiranji patari, Yehova?Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?

2. Podzikuza woipa apsereza waumphawi;Agwe m'ciwembu anapanganaco.

3. Pakuti woipa adzitamira cifuniro ca moyo wace,Adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.

4. Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yace, akuti, Sadzafunsira.Malingaliro ace onse akuti, Palibe Mulungu.

Masalmo 10