1. Muimiranji patari, Yehova?Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?
2. Podzikuza woipa apsereza waumphawi;Agwe m'ciwembu anapanganaco.
3. Pakuti woipa adzitamira cifuniro ca moyo wace,Adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.
4. Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yace, akuti, Sadzafunsira.Malingaliro ace onse akuti, Palibe Mulungu.