Marko 5:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo masiku onse, usiku ndi usana, anakhala m'manda ndi m'mapiri, napfuula, nadzitematema ndi miyala.

6. Ndipo pakuona Yesu kutali, anathamanga, namgwadira Iye;

7. ndipo anapfuula ndi mau olimba, nanena, Ndiri ndi ciani ine ndi Inu, Yesu Mwana wa Mulungu Wamkurukuru? Ndikulumbirirani pa Mulungu, msandizunze.

8. Pakuti ananena kwa iye, Turuka iwe, mzimu wonyansa, kwa munthuyu.

9. Ndipo anamfunsa, Dzina lako ndani? Ndipo ananena kwa Iye, Dzina langa ndine Legio; cifukwa tiri ambiri.

Marko 5