Marko 5:22-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo anadzako mmodzi wa akuru a sunagoge, dzina lace Yairo; ndipo pakuona Iye, anagwada pa mapazi ace, nampempha kwambiri,

23. nanena, kuti, Kamwana kanga kabuthu kalimkutsirizika; ndikupemphani Inu mufikeko, muike manja anu pa iko, kuti kapulwnuke, ndi kukhala ndi moyo.

24. Ndipo ananka naye pamodzi; ndipo khamu lalikuru linamtsata Iye, ndi kumkanikiza Iye.

Marko 5