22. Ndipo Yesu anayankha nanena nao, Khulupirirani Mulungu,
23. Ndithu ndinena ndi inu, kuti, Munthu ali yense akanena ndi phiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m'nyanja; wosakayika mumtima mwace, koma adzakhulupirira kuti cimene acinena cicitidwa, adzakhala naco.
24. Cifukwa cace ndinena ndi inu, Zinthu ziri zonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.
25. Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, kholulukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhulolukire inu zolakwa zanu.
27. Ndipo iwo anadzanso ku Yerusalemu; ndipo m'mene Iye anali kuyenda m'Kacisi, anafika kwa Iye ansembe akuru, ndi alembi ndi akuru;