Marko 11:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Iye analowa m'Yerusalemu, m'Kacisi; ndipo m'mene anaunguza zinthu zonse, popeza ndi madzulo, anaturuka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwoo.

12. Ndipo m'mawa mwace, ataturuka ku Betaniya, Iye anamva njala.

13. Ndipo anaona mkuyu kutali, uli ndi masamba; ndipo anadza Iye, kuti kapena akapezapo kanthu: ndipo m'mene anafikako anapeza palibe kanthu koma masamba okha; pakuti siinali nyengo yace ya nkhuyu.

14. Ndipo anayankha nanena ndi uwo, Munthu sadzadyanso zipatso zako nthawi zonse. Ndipo ophunzira ace anamva,

Marko 11