4. Ndipo anati, Mose analola kulembera kalata wakulekanira, ndi kumcotsa.
5. Koma Yesu anati kwa iwo, Cifukwa ca kuuma kwa mitima yanu anakulemberani lamulo ili.
6. Koma kuyambira pa ciyambi ca malengedwe anawapanga mwamuna ndi mkazi.
7. Cifukwa cace mwamuna adzasiya atate wace ndi amai wace, ndipo adzaphatikizana ndi mkazi wace;
8. ndipo awiriwa adzakhala thupi limodzi: kotero kuti salinso awiri, koma thupi limodzi.