Macitidwe 8:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo Simoni mwini wace anakhulupiranso: ndipo m'mene anabatizidwa, anakhalira ndi Filipo; ndipo pakuona zizindikilo ndi mphamvu zazikuru zirikucitika, anadabwa.

14. Koma pamene atumwi a ku Yerusalemu anamva kuti Samariya adalandira mau a Mulungu, anawatumizira Petro ndi Yohane;

15. amenewo, m'mene adatsikirako, anawapempherera, kuti alandire Mzimu Woyera:

16. pakuti kufikira pamenepo nkuti asanagwe pa wina mmodzi wa iwo; koma anangobatizidwam'dzina la Ambuye Yesu.

17. Pamenepo anaika manja pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.

18. Koma pakuona Simoni kuti mwa kuika manja a atumwi anapatsidwa Mzimu Woyera, anawatengera ndalama,

Macitidwe 8