20. Nyengo yomweyo anabadwa Mose, ndiye wokoma ndithu; ndipo anamlera miyezi itatu m'nyumba ya atate wace:
21. ndipo pakutayika iye, anamtola mwana wamkazi wa Farao, namlera akhale mwana wace.
22. Ndipo Moseanaphunzira nzeru zonse za Aaigupto; nali wamphamvu m'mau ace ndi m'nchito zace.
23. Koma pamene zaka zace zinafikira ngati makumi anai, kunalowa mumtima mwace kuzonda abale ace ana a Israyeli,