Macitidwe 28:6-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma anayesa kuti adzatupa, kapena mwini wace kugwa kufa pomwepo; koma m'mene adalindira nthawitu, naona kuti sikunampweteka, anapindula, nati, Ndiye Mulungu.

7. Koma pafupt pamenepo panali minda, mwini wace ndiye mkulu cisumbuco, dzina lace Popliyo; amene anatilandira ife, naticereza okoma masiku atatu.

8. Ndipo kunatero kuti atate wace wa Popliyo anagona wodwala nthenda ya malungo ndi kamwazi. Kwa iyeyu Paulo analowa, napemphera, naika manja pa iye, namciritsa.

Macitidwe 28