Macitidwe 28:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo itapita miyezi itatu tinayenda m'ngalawa ya ku Alesandriya, idagonera nyengo ya cisanu kucisumbuko, cizindikilo cace, Ana-a-mapasa.

12. Ndipo pamene tinakoceza ku Surakusa, tinatsotsako masiku atatu.

13. Ndipo pocokapo tinapaza ntifika ku Regio; ndipo litapita tsiku limodzi unayamba mwela, ndipo m'mawa mwace tinafika ku Potiyolo:

14. pamenepo tinakomana ndi abale, amene anatiumirira tikhale nao masiku asanu ndi awiri; ndipo potero tinafika ku Roma.

15. Kucokera kumeneko abalewo, pakumva za ife, anadza kukomana nafe ku Bwalo la Apiyo, ndi ku Nyumba za Alendo Zitatu; ndipo pamene Paulo anawaona, anayamika Mulungu, nalimbika mtima.

Macitidwe 28