Macitidwe 21:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. ndipo anamva za iwe, kuti uphunzitsa Ayuda onse a ku amitundu apatukane naye Mose, ndi kuti asadule ana ao, kapena asayende monga mwa miyambo.

22. Nciani tsono? adzamva ndithu kuti wafika.

23. Cifukwa cace ucite ici tikuuza iwe; tiri nao amuna anai amene anawinda;

24. amenewa uwatenge nudziyeretse nao pamodzi, nuwalipirire, kati amete mutu; ndipo adzadziwa onse kuti zomveka za iwe nzacabe, koma kuti iwe wekhaoso uyenda molunjika, nusunga cilamulo.

Macitidwe 21