Macitidwe 17:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo anabvuta anthu, ndi akuru a mudzi, pamene anamva zimenezi.

9. Ndipo pamene analandira cikole kwa Yasoni ndi enawo, anawamasula.

10. Pomwepo abale anatumiza Paulo ndi Sila usiku kunka ku Bereya; pamene iwo anafika komweko analowa m'sunagoge wa Ayuda.

11. Amenewa anali mfulu koposa a m'Tesalonika, popeza analandira mau ndi kufunitsa kwa mtima wonse, nasanthula m'malembo masiku onse, ngati zinthu zinali zotero.

12. Ndipo ambiri a iwo anakhulupira; ndi akazi a Cihelene omveka, ndi amuna, osati owerengeka.

13. Koma pamene Ayuda a ku Tesalonika anazindikira kuti mau a Mulungu analalikidwa ndi Paulo ku Bereyanso, anadza komwekonso, nautsa, nabvuta makamu.

Macitidwe 17