Macitidwe 16:30-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. nawaturutsira iwo kunja, nati, Ambuye, ndicitenji kuti ndipulumuke?

31. Ndipo iwo anati, Ukhulupirire Ambuye Yesu, ndipo udzapulumuka, iwe ndi apabanja ako.

32. Ndipo anamuuza iye mau a Ambuye, pamodzi ndi onse a pabanja pace.

33. Ndipo anawatenga ora lomwelo la usiku, natsuka mikwingwirima yao; nabatizidwa pomwepo, iye ndi a pabanja pace.

34. Ndipo anakwera nao kunka kunyumba kwace, nawakhazikira cakudya, nasangalala kwambiri, pamodzi ndi a pabanja pace, atakhulupirira Mulungu.

35. Kutaca, oweruza anatumiza akapitao, kuti, Mukamasule anthu aja.

Macitidwe 16