27. Koma Ine ndinena ndi inu zoonadi, Kuli ena a iwo akuimirira pano, amene sadzalawatu imfa, kufikira kuti adzaona Ufumu wa Mulungu.
28. Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m'phiri kukapemphera.
29. Ndipo m'kupemphera kwace, maonekedwe a nkhope yace anasandulika, ndi cobvala cace cinayera ndi kunyezimira.
30. Ndipo onani, analikulankhulana nayeamuna awiri, ndiwo Mose ndi Eliya;
31. amene anaonekera m'ulemerero, nanenaza kumuka kwace kumene iye ati adzatsiriza ku Yerusalemu.