Luka 7:45-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Sunandipatsa mpsompsono wa cibwenzi; koma uyu sanaleka kupsompsonetsa mapazi anga, cilowere muno Ine.

46. Sunandidzoza mutu wanga ndi mafuta; koma nyu anadzoza mapazi anga ndimafuta onunkhira bwmo.

47. Cifukwa cace, ndinena kwa iwe, Macimo ace, ndiwo ambiri, akhululukidwa; cifukwa anakonda kwambiri; koma munthu amene anamkhululukira pang'ono, iye akonda pang'ono.

48. Ndipo anati kwa mkazi, Macimo ako akhululukidwa.

Luka 7