45. Sunandipatsa mpsompsono wa cibwenzi; koma uyu sanaleka kupsompsonetsa mapazi anga, cilowere muno Ine.
46. Sunandidzoza mutu wanga ndi mafuta; koma nyu anadzoza mapazi anga ndimafuta onunkhira bwmo.
47. Cifukwa cace, ndinena kwa iwe, Macimo ace, ndiwo ambiri, akhululukidwa; cifukwa anakonda kwambiri; koma munthu amene anamkhululukira pang'ono, iye akonda pang'ono.
48. Ndipo anati kwa mkazi, Macimo ako akhululukidwa.