26. ndipo Eliya sanatumidwa kwa mmodzi wa iwo, koma ku Sarepta wa ku Sidoniya, kwa mkazi wamasiye.
27. Ndipo munali akhate ambiri m'Israyeli masiku a Elisa mneneri; ndipo palibe mmodzi wa iwo anakonzedwa, koma Namani yekha wa ku Suriya.
28. Ndipo onse a m'sunagogemo anadzala ndi mkwiyo pakumva izi;