Luka 24:34-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. nanena, Ambuye anauka ndithu, naonekera kwa Simoni.

35. Ndipo iwo anawafotokozera za m'njira, ndi umo anadziwika nao m'kunyema kwa mkate.

36. Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.

37. Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.

38. Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji obvutika? ndipo matsutsano am auka bwanji m'mtima mwanu?

Luka 24