34. nanena, Ambuye anauka ndithu, naonekera kwa Simoni.
35. Ndipo iwo anawafotokozera za m'njira, ndi umo anadziwika nao m'kunyema kwa mkate.
36. Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.
37. Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.
38. Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji obvutika? ndipo matsutsano am auka bwanji m'mtima mwanu?