Luka 23:45-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Ndipo nsaru yocinga ya m'Kacisi inang'ambika pakati.

46. Ndipo pamene Yesu anapfuula ndi mau akuru, anati, 1 Atate, m'manja mwanu ndipereka mzimu wanga. Ndipo pakutero anapereka mzimu wace.

47. Ndipo 2 pamene kenturiyo anaona cinacitikaco, analemekeza Mulungu, nanena, Zoonadi munthu uyu anali wolungama.

48. Ndipo makamu onse osonkhana kudzapenya ici, pamene anaona zinacitikazo, anapita kwao ndi kudziguguda pacifuwa.

Luka 23