Luka 22:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo anati kwa iwo, Ndinalakalaka ndithu kudya Paskha uwu pamodzi ndinu, ndisanayambe kusautsidwa;

16. pakuti ndinena ndi inu, sindidzadya kufikira udzakwaniridwa mu Ufumu wa Mulungu.

17. Ndipo analandira cikho, ndipo pamene adayamika, anati, Landirani ici, mucigawane mwa inu nokha;

18. pakuti ndinena kwa inu, kuyambira tsopano Ine sindidzamwako cipatso ca mpesa, kufikira Ufumu wa Mulungu udzafika.

Luka 22