23. Koma pakumva izi anagwidwa naco cisoni cambiri; pakuti anali mwini cuma cambiri.
24. Ndipo Yesu pomuona iye anati, Ha! nkubvutika nanga kwa anthu eni cuma kulowa Ufumu wa Mulungu!
25. Pakuti nkwapafupi kwa ngamila apyole diso la singano koma kwa munthu mwini cuma, kulowa Ufumu wa Mulungu nkwapatali.
26. Koma akumvawo anati, Tsono ndani angathe kupulumutsidwa?