Luka 17:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo kunali, pakumuka ku Yerusalemu iye analikupita pakati pa Samariya ndi Galileya.

12. Ndipo m'mene analowa iye m'mudzi wina, anakomana naye amuna khumi akhate, amene anaima kutali;

13. ndipo iwo anakweza mau, nanena, Yesu, Mbuye, muticitire cifundo.

14. Ndipo pakuwaona anati kwa iwo, Pitani, kadzionetseni nokha kwa ansembe. Ndipo kunali, m'kumuka kwao, anakonzedwa.

15. Ndipo mmodzi wa iwo, pakuona kuti anaciritsidwa, anabwerera m'mbuyo, nalemekeza Mulungu ndi mau akuru;

16. ndipo anagwa nkhope yace pansi ku mapazi ace, namyamika iye; ndipo anali Msamariya ameneyo.

Luka 17