Luka 15:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma amisonkho onse ndi anthu ocimwa analikumyandikira kudzamva iye.

2. Ndipo Afarisi ndi alembi anadandaula nati, Uyu alandira anthu ocimwa, nadya nao.

3. Koma anati kwa iwo fanizo ili, nanena,

4. Munthu ndani wa inu ali nazo nkhosa makumikhumi, ndipo pakutayika imodzi ya izo, sasiya nanga m'cipululu zinazo makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi zinai, nalondola yotayikayo kufikira aipeza?

Luka 15