Luka 12:48-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

48. Koma 5 iye amene sanacidziwa, ndipo anazicita zoyenera mikwapulo, adzakwapulidwa pang'ono. Ndipo kwa munthu ali yense adampatsa zambiri, kwa iye adzafuna zambiri; ndipo amene anamuikizira zambiri, adzamuuza abwezere zoposa.

49. Ine ndinadzera kuponya mota pa dziko lapansi; ndipo ndifunanji, ngati unatha kuyatsidwa?

50. Koma ndiri ndi ubatizo ndikabatizidwe nao; ndipo ndikanikizidwa Ine kufikira ukatsirizidwa!

Luka 12