Luka 1:67-71 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

67. Ndipo atate wace Zakariya anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nanenera za Mulungu, nati,

68. Wolemekezeka Ambuye, Mulungu wa Israyeli;14 Cifukwa iye anayang'ana, nacitira anthu ace ciombolo,

69. Ndipo iye anatikwezera ife nyanga ya cipulumutso,Mwa pfuko la Davine mwana wace,

70. 15 (Monga iye analankhula ndi m'kamwa mwa aneneri ace oyera mtima, a kale lomwe),

71. Cipulumutso ca adani athu, ndi pa dzanja la anthu onse amene atida ife;

Luka 1