46. 3 Ndipo Mariya anati,Moyo wanga ulemekeza Ambuye,
47. Ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
48. Cifukwa iye anayang'anira umphawi wa mdzakazi wace;Pakuti taonani, kuyambira tsopano, anthu a mibadwo yonse adzandichula ine wodala.
49. Cifukwa iye Wamphamvuyo anandicitira ine zazikuru;4 Ndipo dzina lace liri loyera.