Luka 1:37-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Cifukwa 1 palibe mau amodzi akucokera kwa Mulungu adzakhala opanda mphamvu.

38. Ndipo Mariya anati, Onani, mdzakazi wa Ambuye; kukhale kwa ine monga mwa mau anu. Ndipo mngelo anacoka kwa iye.

39. Ndipo Mariya ananyamuka masiku amenewa, namuka ndi cangu ku dziko la mapiri ku mudzi wa Yuda;

40. nalowa m'nyumba ya Zakariya, nalankhula Elisabeti.

Luka 1