Levitiko 5:18-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Nadze nayo kwa wansembe nkhosa yamphongo yopanda cirema ya m'khola lace, monga umayesa mtengo wace, ikhale nsembe yoparamula; ndipo wansembeyo amcitire comtetezera cifukwa ca kusacimwa dala kwace, osakudziwa; ndipo adzakhululukidwa.

19. Iyo ndiyo nsembe yoparamula; munthuyu anaparamula ndithu pamaso pa Yehova.

Levitiko 5