Levitiko 27:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo cikakhala ca nyama imene anthu amabwera nayo ikhale copereka ca Yehova, zonse zotere munthu akazipereka kwa Yehova zikhale zopatulika.

10. Asaisinthe, yokoma m'malo mwa yoipa, kapena yoipa m'malo mwa yokoma; ndipo akasinthadi nyama m'malo mwa inzace, pamenepo iyo ndi yosinthikayo zikhale zopatulika.

11. Ndipo cikakhala ca nyama yodetsa, imene sabwera nayo ikhale copereka ca Yehova, aike nyamayi pamaso pa wansembe;

12. ndipo wansembeyo aiyese mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga uiyesa wansembewe, momwemo.

13. Ndipo akaiombola ndithu, pamenepo aonjezepo limodzi la magawo asanu la mtengo wace.

14. Munthu akapatula nyumba yace ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe aziiyesa mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga wansembeyo aiyesa, ikhale momwemo.

Levitiko 27