Levitiko 25:39-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo mbale wako akasaukira cuma, ndi kudzigulitsa kwa iwe; usamamgwiritsa nchito monga kapolo;

40. azikhala nawe ngati wolipidwa nchito, ngati munthu wokhala nawe; akutumikire kufikira caka coliza lipenga.

41. Pamenepo azituruka kukucokera, iye ndi ana ace omwe, nabwerere ku mbumba yace; abwerere ku dziko lao lao la makolo ace.

42. Pakuti iwo ndiwo atumiki anga, amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; asamawagulitsa monga amagulitsa kapolo.

43. Usamamweruza momzunza; koma uope Mulungu wako.

44. Kunena za kapolo wako wamwamuna, kapena wamkazi amene ukhala nao; azikhala a amitundu akuzungulira inu, kwa iwowa muzigula akapolo amuna ndi akazi.

45. Muwagulenso ana a alendo akukhala mwa inu, a iwowa ndi a mabanja ao akukhala nanu, amene anabadwa m'dziko lanu; ndipo adzakhala anu anu.

46. Ndipo muwayese colowa ca ana anu akudza m'mbuyo, akhale ao ao; muwayese akapolo kosatha; koma za abale anu, ana a Israyeli, musamalamulirana mozunza.

Levitiko 25