7. Tsiku lace loyamba mukhale nao msonkhano wopatulika; musamagwira nchito ya masiku ena.
8. Koma mubwere nayo kwa Yehova nsembe yamoto masiku asanu ndi awiri; pa tsiku lacisanu ndi ciwiri pakhale msonkhano wopatulika; musamacita nchito ya masiku ena.
9. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
10. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mutakalowa m'dziko limene ndikupatsani, ndi kuceka dzinthu zace, pamenepo muzidza nao mtolo wa zipatso zoyamba za masika anu kwa wansembe;
11. ndipo iye aweyule mtolowo pamaso pa Yehova, ulandirikire inu, tsiku lotsata sabata wansembe aweyule.