Levitiko 23:20-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndi wansembe awaweyule, pamodzi ndi mkate wa zipatso zoyamba, nsembe yoweyula pamaso pa Yehova, pamodzi ndi ana a nkhosa awiriwo; zikhale zopatulikira Yehova, kuti zikhale za wansembe.

21. Ndipo mulalikire tsiku lomwelo; kuti mukhale nao msonkhano wopatulika; musamagwira nchito ya masiku ena; ndilo lemba losatha m'nyumba zanu zonse, mwa mibadwo yanu yonse.

22. Ndipo pakukolola dzinthu za m'dziko mwanu, usamakololetsa m'mphepete mwa munda wako, nusamakunkha khunkha; uzisiyire wosauka ndi mlendo; Ine ndine Yehova Mulungu wako.

23. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

24. Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzipumula, ndiko cikumbutso ca kuliza malipenga, msonkhano wopatulika.

25. Musamagwira nchito ya masiku ena; mubwere nayo nsembe yamoto ya Yehova.

26. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

27. Komatu, tsiku lakhumi la mwezi uwu wacisanu ndi ciwiri, ndilo tsiku la citetezero; mukhale nao msonkhano wopatulika, ndipo mudzicepetse; ndi kubwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova.

28. Musamagwira nchito iri yonse tsiku limenelo; pakuti ndilo tsiku la citetezero, kucita cotetezera inu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

29. Pakuti munthu ali yense wosadzicepetsa tsiku limenelo, amsadze kwa anthu a mtundu wace.

30. Ndi munthu ali yense wakugwira nchito iri yonse tsiku limenelo, ndidzaononga munthuyo pakati pa anthu a mtundu wace.

31. Musamagwira nchito iri yonse; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu, m'nyumba zanu zoo nse.

32. Likhale ndi inu Sabata lakupumula; ndipo mudzicepetse; tsiku lacisanu ndi cinai madzulo, kuyambira madzulo kufikira madzulo musunge Sabata lanu.

33. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

34. Nena ndi ana a Israyeli, kuti, Tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uno wacisanu ndi ciwiri pali madyerero a misasa a Yehova, masiku asanu ndi awiri.

35. Tsiku loyamba likhale msonkhano wopatulika, musamagwira nchito ya masiku ena.

36. Masiku asanu ndi awiri mubwere nayo nsembe yamoto kwa Yehova; tsiku lacisanu ndi citatu mukhale nao msonkhano wopatulika; ndipo mubwere nayo nsembe yamoto kwa Yehova; ndilo lotsirizira; musamagwira nchito ya masiku ena.

37. Izi ndi nyengo zoikika za Yehova, zimene muzilalikira zikhale masonkhano opatulika, kukabwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova, nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa, nsembe yophera, ndi nsembe yothira, yonse pa tsiku lace lace;

38. pamodzi ndi masabata a Yehova, ndi pamodzi ndi mphatso zanu, ndi pamodzi ndi zoo winda zanu zonse, ndi pamodzi ndi zopereka zaufulu zanu, zimene muzipereka kwa Yehova.

Levitiko 23