Levitiko 22:27-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. kuyambira tsiku lacisanu ndi citatu ndi m'tsogolo mwace, idzalandirika ngati copereka nsembe yamoto ya Yehova.

28. Koma musamaipha ng'ombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wace tsiku limodzimodzi.

29. Ndipo mukamaphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandirike.

30. Idyedwe tsiku lomwelo; musamasiyako kufikira m'mawa; Ine ndine Yehova.

31. Potero muwasunge malamulo anga, ndi kuwacita; Ine ndine Yehova.

32. Musamaipsa dzina langa loyera; koma ndikhale woyera pakati pa ana a Israyeli; Ine ndine Yehova wakukupatulani,

Levitiko 22