Levitiko 21:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Wa mbeu ya Aroni wansembe asayandikize mmodzi wokhala naco cirema, kupereka nsembe zamoto za Yehova; ali naco cirema asayandikize kupereka cakudya ca Mulungu wace.

22. Adye cakudya ca Mulungu wace, copatulikitsa, ndi copatulika;

23. koma asafike ku nsaru yocinga, asayandikize ku guwa la nsembe, popeza ali naco cirema; kuti angaipse malo anga opatulika; popeza Ine ndine Yehova wakuwapatula.

24. Momwemo Mose ananena ndi Aroni, ndi ana ace amuna, ndi ana onse a Israyeli.

Levitiko 21