13. Ndipo adzitengere mkazi akali namwali.
14. Mkazi wamasiye, kapena womleka, kapena woipsidwa, wacigololo, oterewa asawatenge; koma azitenga namwali wa anthu a mtundu wace akhale mkazi wace.
15. Asaipse mbeu yace mwa anthu a mtundu wace; popeza Ine ndine Yehova wakumpatula iye.
16. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
17. Nena ndi Aroni, kuti, Ali yense wa mbeu zako mwa mibadwo yao wakukhala naco cirema, asayandikize kupereka mkate wa Mulungu wace.
18. Pakuti munthu ali yense wokhala naco cirema, asayandikize; wakhungu, kapena wotsimphina, kapena wopunduka mph uno, kapena wamkuru ciwalo,
19. kapena munthu wopunduka phazi kapena wopunduka dzanja,