Levitiko 20:12-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Munthu akagona ndi mpongozi wace, awaphe onse awiri; acita cisokonezo; mwazi wao ukhale pamtu pao.

13. Munthu akagonana ndi mwamuna mnzace, monga amagonana ndi mkazi, acita conyansa onse awiri; awaphe ndithu; mwazi wao ukhale pamtu pao.

14. Munthu akatenga mkazi pamodzi ndi mai wace cocititsa manyazi ici; aziwatentha ndi moto, iye ndi iwowa; kuti pasakhale cocititsa manyazico pakati pa inu.

Levitiko 20