Levitiko 19:23-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo mukadzalowa m'dzikomo, ndi kubzalamitengo yamitundumitundu ikhale ya cakudya, muziyese zipatso zao monga kusadulidwa kwao; zaka zitatu muziyese zosadulidwa; zisadyedwa.

24. Koma caka cacinai zipatso zace zonse zikhale zopatulika, za kumlemekeza nazo Yehova.

25. Caka cacisanu muzidya zipatso zace, kuti zobala zace zikucurukireni inu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

26. Musamadya kanthu ndi mwazi wace; musamacita nyanga, kapena kuombeza ula.

27. Musamameta mduliro, kapena kusenga m'mphepete mwa ndebvu zanu,

28. Musamadziceka matupi anu cifukwa ca akufa, kapena kutema mpbini; Ine ndine Yehova.

29. Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumcititsa cigololo; lingadzale ndi cigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zocititsa manyazi.

Levitiko 19