Levitiko 19:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo adze nayo nsembe yace yoparamula kwa Yehova, ku khomo la cihema cokomanako, ndiyo nkhosa yamphongo ikhale nsembe yoparamula.

22. Ndipo wansembe acite comtetezera ndi nkhosa yamphongo ya nsembe yoparamula pamaso pa Yehova, cifukwa ca kucimwa adacimwaku; ndipo adzakhululukidwa cifukwa ca kucimwa kwace adacimwaku.

23. Ndipo mukadzalowa m'dzikomo, ndi kubzalamitengo yamitundumitundu ikhale ya cakudya, muziyese zipatso zao monga kusadulidwa kwao; zaka zitatu muziyese zosadulidwa; zisadyedwa.

24. Koma caka cacinai zipatso zace zonse zikhale zopatulika, za kumlemekeza nazo Yehova.

Levitiko 19