Levitiko 18:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Usamabvula mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wako, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wako; pakuti thupi lao ndi lako.

11. Usamabvula mwana wamkazi wa mkazi wa atate wako, amene anambala atate wako, ndiye mlongo wako.

12. Usamabvula mlongo wa atate wako; ndiye wa cibale ca atate wako.

13. Usamabvula mbale wa mai wako; popeza ndiye mbale wa mai wako.

14. Usamabvula mbale wa atate wako; usamasendera kwa mkazi wace; ndiye mai wako.

15. Usamabvula mpongozi wako; ndiye mkazi wa mwana wamwamuna wako; usamambvula.

16. Usamabvula mkazi wa mbale wako; ndiye thupi la mbale wako.

17. Usamabvula mkazi ndi mwana wamkazi wace; usamatenga mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wace, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wace kumbvula; ndiwo abale; cocititsa manyazi ici.

Levitiko 18