33. Ndipo acite cotetezera malo opatulikatu, natetezere cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe; momwemo atetezerenso ansembe, ndi anthu onse a msonkhanowo.
34. Ndipo ici cikhale kwa inu lemba losatha, kucita cotetezera ana a Israyeli, cifukwa ca zocimwa zao zonse, kamodzi caka cimodzi. Ndipo anacita monga Yehova adauza Mose.